Mawu a M'munsi
a Apa Yehova ankalankhula ndi anthu a mu ufumu wakumpoto wa Isiraeli wa mafuko 10. Pamene Yeremiya ankapereka uthengawu n’kuti anthu amenewa atakhala mu ukapolo kudziko la eni kwa zaka pafupifupi 100. Ndipo Yeremiya anasonyeza kuti pofika m’nthawi yake, mtunduwo unali usanalapebe. (2 Maf. 17:16-18, 24, 34, 35) Komabe, munthu aliyense payekha akanatha kubwerera kwa Mulungu ngakhalenso kubwerera kudziko lakwawo kuchoka ku ukapolo.