Mawu a M'munsi
b Yesaya ananena ulosi wopita kwa anthu omwe sakanatha kukwatira m’masiku ake, amenenso sankaloledwa kuchita nawo zinthu zina polambira Mulungu m’nthawi ya Aisiraeli. Iye analosera kuti ngati anthuwo angapitirize kukhalabe omvera, adzapatsidwa zinthu “zabwino kuposa ana aamuna ndi aakazi,” zomwe ndi “dzina limene silidzatha mpaka kalekale” m’nyumba ya Mulungu.—Yes. 56:4, 5.