Mawu a M'munsi
b Tiyenera kudziwa kuti magaziniyi, Bapteste komanso Rose sankatsutsa zoti zinthu zinachita kusintha kuchokera ku zinthu zina. Mfundo yawo yaikulu inali yakuti zimene Darwin ananena zoti zamoyo zinachokera ku chinthu chimodzi n’zopanda umboni. Koma asayansi ngati amenewa akufufuzabe njira zina zofotokozera kuti zimene amakhulupirira, zoti zamoyo zinasintha kuchokera ku zinthu zina, ndi zoona.