Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO

Mawu a M'munsi

a “Mawu achifatse apansipansi” amenewa ayenera kuti anali a mngelo amene anagwiritsidwanso ntchito kunena “mawu a Yehova” amene ali palemba la 1 Mafumu 19:9. Pa vesi 15 mngelo ameneyu anangotchulidwa kuti “Yehova.” Zimenezi zingatikumbutse mngelo yemwe Yehova anamugwiritsira ntchito kutsogolera Aisiraeli m’chipululu. Ponena za mngelo ameneyu, Mulungu anati: “Dzina langa lili mwa iye.” (Eks. 23:21) Ngakhale kuti Baibulo silinena mwatchutchutchu kuti mngelo amene analankhula ndi Eliya anali Yesu, mfundo yofunika kuidziwa ndi yakuti Yesu asanabwere padziko lapansi, Yehova ankamugwiritsa ntchito monga “Mawu,” kapena kuti Womulankhulira.—Yoh. 1:1.

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena