Mawu a M'munsi
c M’mwezi wa June, chaka cha 1880, magazini ya Zion’s Watch Tower inafotokoza kuti a 144,000 adzakhala anthu ochokera mu mtundu wachiyuda okha amene adzaphunzire choonadi pofika mu 1914. Koma chakumapeto kwa chaka cha 1880, panatulukanso nkhani ina imene inasintha zomwe ankakhulupirirazo ndipo inafotokoza zofananako ndi zimene timakhulupirira masiku ano.