Mawu a M'munsi
a Ayuda ochokera m’madera ena ankafunika kugwiritsa ntchito ndalama zovomerezeka popereka msonkho wapachaka wapakachisi ndipo anthu osintha ndalama ankawalipiritsa akafuna kusintha ndalama zawo kuti apeze ndalama zovomerezekazo. Anthu a m’madera enawa ankafunikanso kugula nyama zoti apereke nsembe. Yesu anatchula amalondawa kuti ndi “achifwamba,” ndipo n’kutheka kuti anawatchula choncho chifukwa choti ankalipiritsa anthu mitengo yokwera kwambiri.