Mawu a M'munsi
a Choncho Yehova ankasiyanitsa mmene anthu ake anachitira ndi nyumba yake yopatulika m’mbuyomo ponena kuti: “Iwo anaipitsa dzina langa loyera chifukwa cha zinthu zonyansa zimene anachita pamene anaika khomo lawo pafupi ndi khomo langa, nʼkuika felemu la khomo lawo pafupi ndi felemu la khomo langa moti pakati pa iwowo ndi ine nʼkungokhala khoma lokha lotisiyanitsa.” (Ezek. 43:8) Kale ku Yerusalemu, mpanda wokha ndi umene unkasiyanitsa kachisi wa Yehova ndi nyumba za anthu. Anthu atasiya kutsatira mfundo zolungama za Yehova, anabweretsa zinthu zonyansa zomwe ndi kulambira mafano pafupi ndi nyumba ya Yehova. Zimenezo zinali zosaloleka.