Mawu a M'munsi
a Lamulo la Hammurabi silinali ndi zopereka zoterozo; ndiponso linalibe lamulo lofanana nalo la ukhondo lomwe linapezeka pakati pa Aigupto akale, ngakhale kuti iwo anapanga mtundu wapamwamba wa mankhwala. Likutero bukhu la Ancient Egypt: “Kugwira matsenga ndi kalongosoledwe ka mankhwala kuli mwaufulu kophatikizidwa [m’nkhani za mankhwala za Aigupto] ndi kulemberedwa mankhwala.” Lamulo la Mulungu, ngakhale kuli tero, linalibe mbali za uchiwanda, linali mwasayansi labwino. Kokha m’nthaŵi zamakono, mwachitsanzo, adokotala awona kufunika kwa kusamba m’manja pambuyo pakukhudza mitembo, chinachake chimene Chilamulo cha Mose chinafuna zaka mazana apita!—Numeri, mutu 19.