Mawu a M'munsi
a Ophunzira Baibulo ambiri amazindikira kuti nthanthi imeneyi njolakwa, popeza kuti Malemba Achigriki, olembedwa m’zaka za zana loyamba C.E., amalemba kukwaniritsidwa kwa maulosi ambiri a Malemba Achihebri, amene mowonekera analembedwa zaka mazana ambiri kalelo. Mwachitsanzo, kukwaniritsidwa kwa m’zaka za zana loyamba kwa tsatanetsatane wa Danieli 9:24-27 kwalembedwa kaya m’Malemba Achigriki kapena ndi akatswiri a mbiri yakale yakudziko.