Mawu a M'munsi
b Pamalo omwe zinthuzi zinachitikira pafupi ndi chimodzi cha zipata za Masada, zidutswa za mapale 11 zinapezedwa, zokhala ndi dzina losemerera lalifupi Lachihebri lolembedwa pa chirichonse. Akatswiri ambiri akulingalira kuti awa angakhale maere amene alozeredwako ndi Josephus. Paphale lina panazokotedwa kuti “Ben Yaʼir,” kutanthauza kuti “mwana wa Jairus.” “Kutumbidwa kwa maere kochitidwa ndi Yadin, kuphatikizapo ena okhala ndi dzina lakuti Ben Jair pa ilo, kuli chitsimikizo chosakaikirika cha mbiri ya Josephus,” watero Louis Feldman mu Josephus and Modern Scholarship.