Mawu a M'munsi
a M’zaka za zana lachitatu C.E., Tertullian ananena kuti akazi “amene amapaka khungu lawo mankhwala, kupaka masaya awo ndi rouge, kupangitsa maso awo kuwonekera kwambiri ndi antimony [yakuda], amamchimwira Iye.” Iye anasulizanso awo amene amasintha mtundu wa tsitsi lawo. Akumagwiritsira ntchito molakwa mawu a Yesu a pa Mateyu 5:36, Tertullian anatsutsa kuti: “Iwo amatsutsa Ambuye! ‘Tawonani!’ iwo amati, ‘mmalo mokhala ndi [tsitsi] loyera kapena lakuda, tikulipanga lathu kukhala lachikasu.’” Iye anawonjezera kuti: “Mungapezedi anthu amene amachita manyazi kuti akalamba, ndipo amayesa kusintha tsitsi lawo la imvi kukhala lakuda.” Kumeneko kunali kulingalira kwaumwini kwa Tertullian. Koma iye ankasokoneza zinthu, popeza kuti mfundo ya mkangano wake wonse inazikidwa pa lingaliro lake lakuti akazi ndiwo anapangitsa kukanidwa kwa anthu, chotero iwo ayenera ‘kuyendayenda monga Hava, akumalira ndi kulapa’ chifukwa cha ‘manyazi a tchimo loyambirira.’ Baibulo silimanena chinthu choterocho; Mulungu anapatsa Adamu mlandu wa kuchimwa kwa anthu.—Aroma 5:12-14; 1 Timoteo 2:13, 14.