Mawu a M'munsi
a Mwachitsanzo, Christine Elizabeth King analemba kuti: “Boma [la Chinazi] linalephera kokha kwa Mboni, poti ngakhale kuti anazipha zikwizikwi, ntchitoyo inapitirizabe ndipo mu May 1945 gulu la Mboni za Yehova lidalipobe, pamene kuli kwakuti National Socialism panalibenso. Ziŵerengero za Mboni zinawonjezereka ndipo sizinalolere molakwa. Gululo linakhala ndi ofera chikhulupiriro ochuluka ndipo linamenyanso mwachipambano nkhondo ya Yehova Mulungu.”—The Nazi State and the New Religions: Five Case Studies in Non-Conformity, tsamba 193.