Mawu a M'munsi
a “‘Dama’ m’lingaliro lotakata, ndipo monga lagwiritsiridwa ntchito pa Mateyu 5:32 ndi 19:9, mwachiwonekere limasonya ku mitundu yambiri yamaunansi akugonana kosaloledwa ndi lamulo kapena koswa lamulo kwakunja kwaukwati. Porneia [liwu Lachigiriki logwiritsidwa ntchito m’malemba amenewo] limaphatikizapo kugwiritsidwa ntchito koipa kwa mpheto kochitidwa ndi munthu mmodzi kapena oposerapo (kaya kukhale mwanjira yachibadwa kapena yoluluzika); ndiponso, payenera kukhala panali chiŵalo china m’chisembwerecho—mwamuna kapena mkazi, kapena nyama.” (Nsanja ya Olonda, September 1, 1983, tsamba 31) Chigololo ndicho: “Kugonana kodzifunira pakati pa munthu wokwatira ndi munthu wina wosakhala mwamuna kapena mkazi wake walamulo.”—The American Heritage Dictionary of the English Language.