Mawu a M'munsi
a Buku lotchedwa A Linguistic Key to the Greek New Testament, lolembedwa ndi Fritz Rienecker, limafotokoza phor·tiʹon kukhala “katundu amene munthu akuyembekezeredwa kunyamula” ndipo limanenanso kuti: “Linagwiritsiridwa ntchito monga mawu a kunkhondo onena za phukusi la munthu kapena katundu wa msilikali.”