Mawu a M'munsi
a Kuvutika kwakukulu kumene Yesu anapirira mwinamwake kungaonedwe m’chenicheni chakuti munthu wangwiroyo anamwalira pambuyo pa maola oŵerengeka chabe pamtengo wozunzirapo, pamene kuli kwakuti ochita zoipa amene anapachikidwa pamodzi naye anafunikira kuthyoledwa miyendo yawo kufulumizitsa imfa yawo. (Yohane 19:31-33) Iwo sanamve kuvutika kwa maganizo ndi kwakuthupi kofanana ndi kumene Yesu anali nako mkati mwa zochitika za kuimbidwa mlandu usiku wonse asanapachikidwe, mwinamwake kufikira pamlingo wakuti sakanathanso kunyamula mtengo wake wozunzirapo.—Marko 15:15, 21.