Mawu a M'munsi
d Mawu akuti “mpaka nthaŵi ya mapeto” angatanthauze “m’nthaŵi ya chitsiriziro.” Liwu lotembenuzidwa pano kuti “mpaka” limaonekera m’malembo Achiaramu pa Danieli 7:25 ndipo pamenepo limatanthauza kuti “m’nthaŵi” kapena “kwa.” Liwulo lili ndi tanthauzo lofananalo m’malembo Achihebri pa 2 Mafumu 9:22, Yobu 20:5, ndi Oweruza 3:26. Komabe, m’matembenuzidwe ochuluka a Danieli 11:35, limamasuliridwa kuti “mpaka,” ndipo ngati liwuli lili lolondola, pamenepo “nthaŵi ya mapeto” yotchulidwa pano iyenera kukhala nthaŵi ya mapeto a chipiriro cha anthu a Mulungu.—Yerekezerani ndi “Your Will Be Done on Earth,” patsamba 286.