Mawu a M'munsi
a M’Chikatolika chiphunzitso choikidwa, mosiyana ndi chiphunzitso wamba, chimanenedwa kukhala chowonadi cholinganizidwa mwaukumu kaya ndi bungwe la chigwirizano cha matchalitchi kapena ndi papa mwa “ukumu [wake] wa kuphunzitsa wosakhoza kulakwa.” Pakati pa ziphunzitso zoikidwa zofotokozedwa motero ndi Tchalitchi cha Katolika, chatsopano kwambiri ndicho cha Kutengeredwa Kumwamba kwa Mariya.