Mawu a M'munsi
a Pamene Yesu amalankhula za Ufumu wokonzedwa “pa chikhazikiro chake cha dziko lapansi” (Mateyu 25:34), ayenera kukhala akusonya nthaŵi ina ya pambuyo pa tchimo loyambalo. Luka 11:50, 51 amagwirizanitsa “kukhazikika kwa dziko lapansi,” kapena kukhazikitsidwa kwa mtundu wa anthu wowomboleka ndi dipo, ndi nthaŵi ya Abele.