Mawu a M'munsi
a Kwenikweni, iwo ananyoza osauka ndi mawu achipongwe akuti “ʽam-ha·ʼaʹrets,” kapena “anthu apansi.” Malinga ndi katsŵiri wina, Afarisi anaphunzitsa kuti munthu sayenera kuikizira chuma kwa anthu ameneŵa, kapena kukhulupirira umboni wawo, kapena kuwachereza monga alendo, kapena kukhala alendo awo, kapenanso kugula zinthu kwa iwo. Atsogoleri achipembedzo ananena kuti kukwatiwa kwa mwana wamkazi wa munthu kwa anthu ameneŵa kukakhala ngati kumpereka ku chilombo ali wonjatidwa ndi wopanda thandizo.