Mawu a M'munsi
b Cha ku ma 760 C.E., gulu lina Lachiyuda lodziŵika monga Akaraiti linafuna kuti anthu amamatire kwambiri ku Malemba. Pokana ulamuliro wa arabi, “Lamulo la Pakamwa,” ndi Talmud, anali ndi chifukwa chokulirapo chotetezerera malembo a Baibulo mosamala kwambiri. Mabanja ena a m’gulu limeneli anakhala Amasoreti okopa malembo mwaukatswiri.