Mawu a M'munsi
a The International Standard Bible Encyclopedia imalongosola kuti: “Akazi sanadye ndi alendo achimuna, ndipo amuna analetsedwa kulankhula ndi akazi. . . . Kucheza ndi akazi poyera kunalidi konyansa.” Mishnah Yachiyuda, mpambo wa ziphunzitso zachirabi, unalangiza kuti: “Musalankhule kwambiri ndi akazi. . . . Munthu amene amalankhula kwambiri ndi akazi amadzibweretsera tsoka ndipo amanyalanyaza kuphunzira Chilamulo ndipo potsirizira adzaloŵa ku Gehena.”—Aboth 1:5.