Mawu a M'munsi
a Onani kuti zimenezi zisanachitike, Yakobo anali atachitapo kanthu kale mwamphamvu kutetezera banja lake pa chisonkhezero cha Akanani. Anamanga guwa la nsembe, limene mosakayikira linamsiyanitsa ndi anansi ake Achikanani. (Genesis 33:20; Eksodo 20:24, 25) Ndiponso, anaimika hema wake kunja kwa mzinda wa Sekemu ndi kukumba chitsime cha iye mwini. (Genesis 33:18; Yohane 4:6, 12) Motero Dina ayenera kukhala atadziŵa bwino za chikhumbo cha Yakobo chakuti asayanjane ndi Akanani.