Mawu a M'munsi
a Mwa kufufuza kwake deralo, katswiri wa zaulimi Walter C. Lowdermilk (woimira Food and Agriculture Organization ya United Nations) anati: “Dzikoli kale linali paradaiso wa zifuyo.” Ndiponso ananena kuti mkhalidwe wake wakunja sunasinthe kwenikweni “chiyambire nthaŵi za Aroma,” ndipo “‘chipululu’ chimene chinakuta dziko limene linali lachonde chinakhalako chifukwa cha munthu, osati chilengedwe.”