Mawu a M'munsi
a Imodzi ya ntchito zazikulu za mzimu wa Mulungu pa Akristu a m’zaka za zana loyamba inali kuwadzoza monga ana olera auzimu a Mulungu ndi abale a Yesu. (2 Akorinto 1:21, 22) Zimenezi zimangochitika kwa ophunzira a Kristu okwanira 144,000. (Chivumbulutso 14:1, 3) Lerolino, Akristu ochuluka apatsidwa chiyembekezo cha moyo wosatha padziko lapansi la paradaiso. Ngakhale kuti sali odzozedwa, iwonso amalandirako chithandizo ndi chitonthozo cha mzimu woyera wa Mulungu.