Mawu a M'munsi
c Nyimbo zina m’buku lathu latsopano la nyimbo, Imbirani Yehova Zitamando, zili ndi mbali zinayi zogwirizana kuti awo amene amatha kuimba tchuni chosiyanacho asangalale nazo. Komabe, nyimbo zambiri azilinganiza kuti zizitsagana ndi piyano ndipo kaimbidwe kake kanakonzedwa kuti zikhalebe ndi tchuni chake cha kumaiko kumene zinachokera. Kudzikonzera manotsi m’nyimbo zolembedwa popanda mbali zake zinayi za tchuni kungachititse kuimba kwathu kumveka kokoma pamisonkhano.