Mawu a M'munsi
a Pano Titus anali kudzapambana basi. Komabe, pazinthu ziŵiri zazikulu, sanakwaniritse cholinga chake. Anawapatsa mwaŵi woti angogonja nadzipereke mwamtendere, koma atsogoleri a mzindawo anakana kwa mtu wa galu. Ndipo pamene makoma a mzindawo anagumulidwa potsirizira pake, analamula kuti kachisi atsale. Koma anatenthedwa yense! Ulosi wa Yesu unasonyeza bwino lomwe kuti Yerusalemu adzasakazidwa ndi kuti kachisi wake adzawonongedwa kotheratu.—Marko 13:1, 2.