Mawu a M'munsi
c Mu 1267, Naḥmanides anafika m’dziko lomwe tsopano limatchedwa Israel. Pazaka zake zomaliza, anachita zambiri. Anadzutsanso Chiyuda nakhazikitsa malo a maphunziro m’Jerusalem. Anamalizanso buku lomasulira Torah, mabuku asanu oyamba a Baibulo, nakhala mtsogoleri wauzimu wa Ayuda mumzinda wakumpoto wa Acre, kumene anafera mu 1270.