Mawu a M'munsi
a Ma Baibulo ena panopa amapereka lingaliro lakuti wokhudza anthu a Mulungu amakhudza, osati diso la Mulungu, koma la Israyeli kapena ngakhale lake iye mwini. Kuphonya kumeneku kunakhalako chifukwa alembi a m’nyengo zapakati amene, poyesa mosokera kukonza mavesi amene iwo anaganiza kuti sanali kupereka ulemu, anasintha vesili. Motero iwo anabisa mphamvu ya chifundo chake cha Yehova.