Mawu a M'munsi
b Nkhani ino ikunena kwambiri za zinenero zomwe zingafotokoze bwino lomwe nkhaniyi koma otembenuza a zinenerozo amalekera dala kutero. Chifukwa cha kuchepa kwa mawu m’zinenero zina, otembenuza amalephera kuchita zambiri. Choncho, alangizi oona mtima achipembedzo adzafotokoza kuti ngakhale kuti wotembenuza anagwiritsira ntchito mawu osiyanasiyana kapena ngakhale kuti anagwiritsira ntchito liwu lokhala ndi matanthauzo ena osakhala a m’Malemba, liwu la m’chinenero choyambirira, neʹphesh, limagwira ntchito kwa anthu ndi nyama zomwe ndipo limatanthauza chinthu chimene chimapuma, kudya, ndipo chimene chingafe.