Mawu a M'munsi
a Chidonati chinali gulu la mpatuko “lachikristu” m’zaka za zana lachinayi ndi lachisanu C.E. Akhulupiriri ake ankati makhalidwe abwino a mtumikiyo ndiwo amapangitsa masakalamenti kukhala oona ndi kuti anthu amachimo aakulu ayenera kuchotsedwa m’tchalitchi. Chiariani chinali gulu “lachikristu” m’zaka za zana lachinayi lomwe silinkavomereza umulungu wa Yesu Kristu. Arius anaphunzitsa kuti Mulungu sanabadwe ndipo alibe chiyambi. Mwana, popeza kuti anabadwa, sangakhale Mulungu monga Atate alili. Mwana sanakhalepo nthaŵi zonse koma kuti analengedwa ndipo ali ndi moyo chifukwa cha chifuniro cha Atate.