Mawu a M'munsi
b Pamene anali m’ndende kachiŵiri ku Roma, Paulo anapempha Timoteo kuti abweretse “mabuku, makamaka zikopa zija zolembedwa.” (2 Timoteo 4:13) Paulo ayenera kuti anali kufuna zigawo za Malemba Achihebri kuti aziwaphunzira m’ndendemo. Mawu akuti “makamaka zikopa zija zolembedwa” angasonyeze kuti panali mabuku agumbwa ndi azikopa omwe.