Mawu a M'munsi
d Kudziŵana kwa Yohane ndi mkulu wa ansembe ndi banja la mkulu wa ansembeyo kukuonekeranso mowonjezereka pambuyo pake m’nkhani yake. Mmodzi mwa akapolo a mkulu wa ansembe atanena kuti Petro ndi mmodzi mwa ophunzira a Yesu, Yohane akufotokoza kuti kapolo ameneyu anali “mbale wake wa uja amene Petro anamdula khutu.”—Yohane 18:26.