Mawu a M'munsi
a Ofufuza ena amanena kuti Yuda anali kugwira mawu buku lopanda umboni lotchedwa kuti Buku la Enoke. Komabe, R. C. H. Lenski akuti: “Tikufunsa kuti: ‘Kodi buku lankhani zosiyanasiyana limeneli, Buku la Enoke, linachokera kuti?’ Buku limeneli linangosonkhanitsa nkhani zosiyanasiyana, ndipo palibe amene angatsimikizire za madeti a zigawo zake zosiyanasiyana . . . ; palibe amene ali ndi umboni wakuti mawu ake ena sanatengedwe kwa Yuda iye mwini.”