Mawu a M'munsi
a Josephus anasimba kuti atangofa Festo, Ananus (Hananiya) wa m’kagulu ka Asaduki anakhala mkulu wa ansembe. Iye anatenga Yakobo, mbale wake wa Yesu mwa atate ena, ndi ophunzira ena napita nawo ku bungwe la Sanhedrin ndipo anaweruzidwa kuti aphedwe ndi kuponyedwa miyala.