Mawu a M'munsi
a Ngakhale kuti Paulo ‘analangiza,’ sizikutanthauza kuti anaika malamulo ake oti aliyense adziwatsatira. M’malo mwake, Paulo anali kungoyang’anira zoperekazo, zochokera kumipingo ingapo. Ndiponso, Paulo ananena kuti aliyense ‘payekha’ anafunikira kupereka “monga momwe anapindula.” M’mawu ena, chopereka chilichonse chinayenera kuperekedwa ndi munthu kwayekha ndiponso modzifunira. Palibe amene anakakamizidwa.