Mawu a M'munsi
a “Zizindikiro za Aroma zinali kusungidwa monga milungu mu akachisi a ku Roma; ndipo anthu ameneŵa akamagonjetsa mitundu ina ulemu wawo pa zizindikirozo unali kuwonjezeka . . . [Kwa asilikali] mwina ndizo zinali chinthu chopatulika koposa padziko lapansi. Msilikali wachiroma anali kulumbira pa chizindikiro chake.”—The Encyclopædia Britannica, 11th Edition.