Mawu a M'munsi
a Malinga ndi kunena kwa buku lakuti The History of the Jewish People in the Age of Jesus Christ (Mbiri ya Ayuda m’Nthaŵi ya Yesu Kristu) (175 B.C.–A.D. 135), lolembedwa ndi Emil Schürer, ngakhale kuti Mishnah sinenapo chilichonse pa mmene Sanihedirini Yaikulu, kapena kuti Sanihedirini ya Mamembala 71 inali kugwirira ntchito, zochita za Masanihedirini ang’onoang’ono, a mamembala 23, zinalongosoledwa mwatsatanetsatane. Ophunzira Chilamulo anali kukamverera milandu yolandira chilango cha imfa imene inali kukambidwa ndi Masanihedirini ang’onoang’ono, kumene anali kuloledwa kulankhula kokha movomereza ndipo osati motsutsa woimbidwa mlanduyo. M’nkhani zosakhudza chilango cha imfa, ankatha kuchita zonse.