Mawu a M'munsi
a Paulo anatchula mawu a pa Habakuku 2:4 monga momwe alili mu Septuagint, imene ili ndi mawu akuti “ngati wina abwerera, moyo wanga ulibe kukondwera mwa iye.” Mawu ameneŵa sakupezeka m’mipukutu yachihebri imene ilipo tsopano. Ena anena kuti Septuagint inazikidwa pa mipukutu yachihebri yakale kwambiri imene kulibenso lerolino. Mulimonse mmene zinalili, Paulo anawaphatikiza pano mawuwo mosonkhezeredwa ndi mzimu woyera wa Mulungu. Chotero mawuwo ndi ouziridwa ndi Mulungu.