Mawu a M'munsi
b Nthaŵi yomaliza pamene Yosefe akutchulidwa mwachindunji ndiyo pamene Yesu wazaka 12 zakubadwa anapezeka m’kachisi. Sizikutchulidwa kuti Yosefe analipo paphwando laukwati ku Kana, kuchiyambiyambi kwa utumiki wa Yesu. (Yohane 2:1-3) Mu 33 C.E., atapachikidwa, Yesu anapereka Mariya m’manja mwa mtumwi wake wokondedwa Yohane kuti am’samalire. Zikuoneka kuti Yesu sakanachita zimenezo zikanakhala kuti Yosefe anali adakali moyo.—Yohane 19:26, 27.