Mawu a M'munsi
a Mawu achigiriki otembenuzidwa kuti “atumiki” angaimire kapolo wopalasa ngalawa yaikulu pogwiritsa ntchito zopalasira zakunthungo m’ngalawamo. Mosiyana ndi zimenezo, “adindo” angapatsidwe maudindo ambiri, mwinamwake kuyang’anira munda waukulu. Komabe, kwa olamulira ambiri, mdindo sanali kum’siyanitsa ndi mtumiki wopalasa ngalawayo.