Mawu a M'munsi
a “Kusiyana kwakukulu [pakati pa Yesu ndi Afarisi] kukuonekera makamaka pa kusiyana kwa mmene anali kum’dziŵira Mulungu. Kwa Afarisi, khalidwe lalikulu la Mulungu ndilo kulamula; koma kwa Yesu, Mulungu ndi wokoma mtima ndiponso wachifundo. N’zoona kuti Afarisi ankavomereza kuti Mulungu ndi wabwino ndiponso wachikondi, koma kwa iwo, Mulungu anasonyeza zimenezi popereka mphatso ya Torah [Chilamulo] ndiponso kukwaniritsa zomwe zili m’Chilamulocho . . . Afarisi ankaona kuumirira mwambo pamodzi ndi malamulo ake otanthauzira chilamulo kukhala njira yokwaniritsira Torah. . . . Kutsindika kwa Yesu malamulo aŵiri onena za chikondi (Mateyu 22:34-40) kuti ndiwo tanthauzo la Chilamulo ndi kukana kwake miyambo ya pakamwa yokhwimitsa zinthu . . . zinam’chititsa kutsutsana ndi kutanthauzira kolakwika kwa Afarisi.”—The New International Dictionary of New Testament Theology.