Mawu a M'munsi
a Khoma lamiyala lalifupi ndilo linkatchinga pakati pa Chipinda cha anthu Akunja ndi chipinda cha m’kati. Nthaŵi ndi nthaŵi pa khoma limeneli ankaikapo zikwangwani zochenjeza. Zina ankazilemba m’Chigiriki ndipo zina m’Chilatini. Ankalembapo kuti: “Wakunja asadutse chotchinga ichi kuloŵa ku malo opatulika. Aliyense wopezeka atachita zimenezi adzaphedwa.”