Mawu a M'munsi
a Petro atapita ku Antiokeya wa ku Suriya, anacheza bwino ndi anthu okhulupirira omwe sanali Ayuda. Koma Akristu achiyuda atafika kuchokera ku Yerusalemu, Petro “anadzibweza, ndi kudzipatula yekha, pakuopa iwo a ku mdulidwe.” Tingathe kuona mmene anthu otembenuka omwe sanali Ayudawo ayenera kuti anakhumudwira pamene mtumwi wolemekezekayo anakana kudya nawo.—Agalatiya 2:11-13.