Mawu a M'munsi
a Yohane, mwana wa Zebedayo, ayenera kuti analondola Yesu atakumana koyamba, ndipo anaona zina zimene Yesu anachita. Mwina ndi zimene zinachititsa Yohane kulemba zinthuzo mogwira mtima kwambiri mu Uthenga wake Wabwino. (Yohane, machaputala 2-5) Koma anadzabwererabe ku ntchito yake ya usodzi kwa nthawi ndithu Yesu asanamuitanenso.