Mawu a M'munsi
a N’kutheka kuti mawu amenewa akunena zimene woyang’anira malo ozungulira kachisi ku Yerusalemu ankachita. M’kati mwa usiku, iye ankayendera kachisiyo kuti aone ngati alonda achilevi, amene ankalondera malo osiyanasiyana pakachisiyo ali m’maso kapena ngati akugona. Mlonda aliyense wopezeka akugona ankamumenya ndi ndodo, ndipo zovala zake ankatha kuzitentha. Ichi chinali chilango chochititsa manyazi.