Mawu a M'munsi
b Baibulo silinena kuti “munga m’thupi” umene Paulo anali nawowu unali chiyani makamaka. N’kutheka kuti mwina unali vuto linalake, monga vuto la maso. N’kuthekanso kuti mawu akuti “munga m’thupi” ankatanthauza atumwi onyenga ndi anthu enanso amene ankatsutsa kuti Paulo anali mtumwi weniweni, n’kumalimbana ndi utumiki wake.—2 Akorinto 11:6, 13-15; Agalatiya 4:15; 6:11.