Mawu a M'munsi
c Anthu ena ophunzira mozama amati kugwa pansi kwa mphetaku n’kutheka kuti sikukutanthauza chabe kufa kwa mphetazo. Amati mawu a Chigirikiwo angathe kutanthauza za kufika pansi kwa mbalameyo ikamatera kuti idye chakudya. Ngati tanthauzo la mawu amenewa lili limeneli, ndiye kuti Mulungu amaona ndiponso amasamalira mbalamezi pa zochitika zawo zonse za tsiku n’tsiku, osati zikangofa chabe ayi.—Mateyu 6:26.