Mawu a M'munsi
a Kale, Mfumu Davide ya Israyeli inalanda Ajebusi phiri la Ziyoni la padziko lapansi pano, n’kulisandutsa likulu la ufumu wake. (2 Samueli 5:6, 7, 9) Inasamutsanso Likasa lopatulika n’kupita nalo komweko. (2 Samueli 6:17) Popeza Likasa linkaimira kukhalapo kwa Yehova, Ziyoni ankatchedwa malo omwe Mulungu ankakhala, zomwe zinachititsa kuti malowa akhale oyenera kuimira kumwamba.—Eksodo 25:22; Levitiko 16:2; Salmo 9:11; Chivumbulutso 11:19.