Mawu a M'munsi
c Chochititsa chidwi n’chakuti Eliya anawauza kuti: “Musasonkhepo moto” pa nsembeyo. Akatswiri ena a Baibulo amati opembedza mafano amenewa nthawi zina ankagwiritsa ntchito maguwa ansembe amene ankakhala ndi bowo kunsi kumene amabisako moto n’cholinga choti anthu aziona ngati kuti milungu yawo ndiyo yayatsa motowo.