Mawu a M'munsi
a Mawu achigiriki amene anawamasulira kuti zinyalala amatanthauza “zinthu zimene zaperekedwa kwa agalu,” “ndowe” kapena “zonyansa za munthu.” Katswiri wina wa Baibulo ananena kuti Paulo anagwiritsa ntchito mawuwa potanthauza “kukaniratu chinthu chopanda ntchito ndiponso chonyansa chimene munthu alibe nacho ntchito.”